2 Samueli 22

Nyimbo yoyamikira ya Davide

1 Ndipo Davide analankhula kwa Yehova mau a nyimbo iyi tsikuli Yehova anampulumutsa m’dzanja la adani ace onse, ndi m’dzanja la Sauli.

2 Ndipo anati:-

Yehova ndiye thanthwe langa, ndi ngaka yanga, ndi mpulumutsi wanga, wangadi;

3 Mulungu wa thanthwe langa, Iye ndidzamkhulupirira;

Cikopa canga, ndi nyanga ya cipulumutso canga, nsanja yanga yaitali, ndi populumukirapo panga;

Mpulumutsi wanga, mundipulumutsa kuciwawa.

4 Ndidzaitanakwa Yehovaamene ayenera timtamande;

Comweco ndidzapulumutsidwa kwa adani anga.

5 Pakuti mafunde a imfa anandizinga,

Mitsinje ya zopanda pace inandiopsa ine.

6 Zingwe za kumanda zinandizingira;

Misampha ya imfa inandifikira ine.

7 M’kusauka kwanga ndinaitana kwa Yehova,

Inde ndinakuwira kwa Mulungu wanga;

Ndipo Iye anamva mau anga ali m’kacisi wace,

Ndi kulira kwanga kunafika ku makutuace.

8 Pomwepo dziko linagwedezeka ndi kunthunthumira.

Maziko a dziko la kumwamba anasunthika

Nagwedezeka, cifukwa iye anakwiya.

9 M’mphuno mwace munaturuka utsi,

Ndi moto woturuka m’kamwa mwace unaononga;

Makala anayaka nao.

10 Anaweramitsa miyambanso, natsika;

Ndipo mdima wandiwe-yani unali pansi pa mapazi ace.

11 Ndipo iye anaberekeka pa Kerubi nauluka;

Inde anaoneka pa mapiko a mphepo,

12 Ndipo anayesa mdimawo ngati mahema omzungulira iye,

Kusonkhana kwa madzi ndi mitambo yocindikira ya mlengalenga.

13 Ceza ca pamaso pace

Makala a mota anayaka,

14 Yehova anagunda kumwamba;

Ndipo Wam’mwambamwamba ananena mau ace.

15 Ndipo iye anatumiza mibvi, nawawaza;

Mphezi, nawaopsa,

16 Pamenepo m’munsi mwa nyanja munaoneka,

Maziko a dziko anaonekera poyera,

Ndi mthonzo wa Yehova,

Ndi mpumo wa mweya wa m’mphuno mwace.

17 Iye anatumiza kucokera kumwamba nanditenga;

Iye ananditurutsa m’madzi akuru;

18 Iye anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu,

Kwa iwo akudana ndi ine; pakuti anandiposa mphamvu,

19 Anandifikira ine tsiku la tsoka langa;

Koma Yehova anali mcirikizo wanga,

20 Iye ananditurutsanso ku malo akuru;

Iye anandipulumutsa, cifukwa akondwera ndi ine.

21 Yehova anandibwezera monga mwa colungama canga;

Monga mwa kuvera kwa manja anga anandipatsa mphotho.

22 Pakuti ndinasunga njira za Yehova,

Osapambukira koipa kusiya Mulungu wanga.

23 Pakuti maweruzo ace onse anali pamaso panga;

Ndipo za malemba ace, sindinawapambukira.

24 Ndinakhalanso wangwiro kwa iye,

Ndipo ndinadzisunga kusacita kuipa kwanga.

25 Cifukwa cace Yehova anandibwezera monga mwa colungama canga;

Monga mwa kuyera kwanga pamaso pace.

26 Ndi acifundo Inu mudzadzionetsa wacifundo,

Ndi munthu wangwiro mudzadzionetsa wangwiro;

27 Ndi oyera mtima mudzadzionetsa woyera mtima;

Ndi otsutsatsutsa mudzadzionetsa wopotoza.

28 Ndipo mudzapulumutsa anthu osautsidwa;

Koma maso anu ali pa odzikuza kuti muwacepetse.

29 Pakuti Inu ndinu nyali yanga, Yehova;

Ndipo Yehova adzaunika mumdima mwanga.

30 Pakuti ndi Inu ndithamangira gulu;

Ndi Mulungu wanga ndilumphira linga.

31 Kunena za Mulungu, njira yace iri yangwiro;

Mau a Yehova anayesedwa; iye ndiye cikopa kwa onse akukhulupirira iye.

32 Pakuti Mulungu ndani, koma Yehova?

Ndipo thanthwe ndani, koma Mulungu wathu?

33 Mulungu ndiye Gnga langa lamphamvu;

Ndipo iye ayendetsa angwiro mu njira yace.

34 Iye asandutsa mapazi ace akunga mapazi a mbawala;

Nandiika pa misanje yanga.

35 Iye aphunzitsa manja anga nkhondo;

Kotero kuti manja anga alifula uta wamkuwa.

36 Ndiponso munandipatsa cikopa ca cipulumutso canu;

Ndi kufatsa kwanu kunandikulitsa.

37 Munakulitsa kulunza kwanga pansi panga,

Ndi mapazi anga sanaterereka.

38 Ndinapitikitsa adani anga, ndi kuwaononga;

Ndiponso sindinabwerera mpaka nditawatha.

39 Ndinawatha ndi kuwapyoza, kuti sakhoza kuuka,

Inde anagwa pansi pa mapazi anga.

40 Pakuti Inu munandimanga m’cuuno ndi mphamvu ya kunkhondo; Munandigonjetsera akundiukira.

41 Munatembenuzitsanso adani anga andipatse mbuyo,

Kuti ndiwalikhe akudana ndi ine.

42 Anayang’ana iwo, koma panalibe wopulumutsa;

Ngakhale kwa Yehova, koma iye sanawayankha.

43 Pomwepo ndinawasansantha asalale ngati pfumbi la padziko,

Ndinawapondereza ngati dothi la m’makwalala.

44 Inunso munandipulumutsa ine pa kulimbana kwa anthu anga;

Munandisunga ndikhale mutu wa amitundu;

Anthu amene sindinawadziwa adzanditsumikira ine.

45 Alendo adzandigonjera ine,

Pakumva za ine, adzandimbera pomwepo.

46 Alendo adzafota,

Nadzabwera ndi kunthunthumira oturuka mokwiririka mwao.

47 Yehova ali ndi moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa;

Ndipo akulitsidwe Mulungu wa thanthwe la cipulumutso canga;

48 Inde Mulungu wakundibwezera cilango ine,

Ndi kundigonjetsera anthu a mitundu.

49 Amene anditurutsa kwa adani anga;

Inde mundikweza ine pamwamba pa iwo akundiukira;

Mundipulumutsa kwa munthu waciwawa.

50 Cifukwa cace ndidzakuongani Yehova, pakati pa amitundu,

Ndipo ndidzayimba zolemekeza dzina lanu.

51 Iye apatsa mfumu yace cipulumutso cacikuru;

Naonetsera cifundo wodzozedwa wace,

Kwa Davide ndi mbeu yace ku nthawi zonse.