Yobu 17

1 Mzimu wanga watha, masiku anga afafanizika,

Kumanda kwandikonzekeratu.

2 Zoonadi, ali nane ondiseka;

Ndi diso langa liri cipenyere m’kundiwindula kwao.

3 Mupatse cigwiriro tsono, mundikhalire cikole Inu nokha kwanu;

Ndani adzapangana nane kundilipirira?

4 Pakuti mwabisira mtima wao nzeru;

Cifukwa cace simudzawakuza.

5 Iye wakupereka mabwenzi ace kuukapolo,

M’maso mwa ana ace mudzada.

6 Anandiyesanso nthanthi za anthu;

Ndipo ndakhala ngati munthu womthira malobvu pankhope pace.

7 M’diso mwanga mucita cizirezire cifukwa ca cisoni,

Ndi ziwalo zanga zonse ziribe cithunzi.

8 Anthu oongoka mtima adzadabwa naco,

Ndi munthu wosalakwa adzadziutsa kumtsotsa wonyoza Mulunguyo.

9 Koma wolungama asungitsa njira yace,

Ndi iye wa manja oyera adzakulabe mumphamvu.

10 Koma bwerani inu nonse, idzani tsono;

Pakuti sindipeza mwa inu wanzeru.

11 Masiku anga apitirira, zolingirira zanga zaduka,

Zace zace zomwe za mtima wanga.

12 Zisanduliza usiku ukhale usana;

Kuunika kuyandikana ndi mdima.

13 Ndikayembekezera kumanda kukhale nyumba yanga;

Ndikayala pogona panga mumdima.

14 Ndikati kwa dzenje, Ndiwe atate wanga;

Kwa mphutsi, Ndiwe mai wanga ndi mlongo wanga;

15 Ciri kuti ciyembekezo canga?

Inde, ciyembekezo canga adzaciona ndani?

16 Cidzatsikira ku mipingiridzo ya kumanda,

Pamene tipumulira pamodzi kupfumbi.