Yobu 23

Yobu abwereza kukana kuti sanacimwa. Mulungu wosadziwika acita cifuniro cace. Kwambiri ocimwa oyenera kulangidwa akhala bwino m’moyo uno

1 Koma Yobu anayankha, nati,

2 Lero lomwe kudandaula kwanga kumawawa;

Kulanga kwanga kuposa kubuula kwanga m’kulemera kwace.

3 Ha! ndikadadziwa kumene ndikampeza Mulungu,

Kuti ndifike ku mpando wace!

4 Ndikadalongosola mlandu wanga pamaso pace,

Ndikadadzaza m’kamwa mwanga ndi matsutsano.

5 Ndikadadziwa mau akadandiyankha ine,

Ndikadazindikira cimene akadanena nane.

6 Akadatsutsana nane kodi mwa mphamvu yace yaikuru?

Iai, koma akadandicherera khutu.

7 Apo woongoka mtima akadatsutsana naye;

Ndipo ndikadapulumuka cipulumukire kwa Woweruza wanga.

8 Taonani, ndikamka m’tsogolo, kulibe Iye;

Kapena m’mbuyo sindimzindikira;

9 Akacita Iye kulamanzere, sindimpenyerera;

Akabisala kulamanja, sindimuona,

10 Koma adziwa njira ndilowayi;

Atandiyesa ndidzaturuka ngati golidi.

11 Phazi langa lagwiratu moponda Iye,

Ndasunga njira yace, wosapambukamo.

12 Sindinabwerera kusiya malamulo a pa milomo yace;

Ndasungitsa mau a pakamwa pace koposa lamulo langa langa.

13 Koma Iye ndiye wa mtima umodzi, adzambweza ndani?

Ndi ici cimene moyo wace ucifuna acicita.

14 Pakuti adzacita condiikidwiratu;

Ndipo zambiri zotere ziri ndi Iye.

15 Cifukwa cace ndiopsedwa pankhope pace;

Ndikalingirira, ndicita mantha ndi Iye.

16 Pakuti Mulungu walefula mtima wanga,

Ndi Wamphamvuyonse wandiopsa.

17 Popeza sindinalikhidwa usanafike mdimawo,

Ndipo sanandiphimbira nkhope yanga ndi mdima wa bii.