Yobu 24

1 Wamphamvuyonse alekeranji kuikiratu nyengo?

Ndi iwo omdziwa alekeranji kudziwa masiku ace?

2 Alipo akusendeza malire;

Alanda gulu la zoweta, nazidyetsa.

3 Akankhizira kwao buru wa amasiye,

Atenga ng’ombe ya mfedwa ikhale cikole.

4 Apambukitsa aumphawi m’njira;

Osauka a padziko abisala pamodzi.

5 Taonani, ngati mbidzi za m’cipululu

Aturukira ku nchito zao, nalawirira nkufuna cakudya;

Cipululu ciwaonetsera cakudya ca ana ao.

6 Atema dzinthu zao m’munda;

Natola khunkha m’munda wampesa wa woipa.

7 Agona amarisece usiku wonse opanda cobvala,

Alibe copfunda pacisanu.

8 Abvumbwa ndi mvula kumapiri,

Nafukata thanthwe posowa pousapo.

9 Akwatula wamasiye kubere,

Natenga cikole cobvala ca osauka;

10 Momwemo ayenda amarisece opanda cobvala,

Nasenza mtolo wa dzinthu ali ndi njala.

11 M’kati mwa malinga a iwo aja ayenga mafuta;

Aponda mphesa moponderamo, namva ludzu.

12 M’mudzi waukuru anthu abuula alinkufa;

Ndi moyo wa iwo olasidwa upfuula;

Koma Mulungu sasamalira coipaco.

13 Iwo ndiwo amene apikisana nako kuunika,

Sadziwa njira zace,

Sasunga mayendedwe ace.

14 Kukaca auka wambanda, napha wosauka ndi waumphawi;

Ndi usiku asanduka mbala.

15 Ndipo diso la wacigololo liyombekezera cisisira,

Ndi kuti, Palibe diso lidzandiona;

Nabvala cophimba pankhope pace.

16 Kuli mdima aboola nyumba,

Usana adzitsekera,

Osadziwa kuunika.

17 Pakuti iwo onse auyesa m’mawa mthunzi wa imfa;

Pakuti adziwa zoopsa za mthunzi wa imfa.

18 Atengedwa ngati coyandama pamadzi;

Gawo lao litembereredwa padziko;

Sadzalunjikanso njira ya minda yamphesa.

19 Cirala ndi dzuwa zitha madzi a cipale cofewa,

Momwemo manda acita nao ocimwa.

20 M’mimba mudzamuiwala; mphutsi zidzamudya mokondwera.

Sadzamkumbukilanso;

Ndipo cosalungama cidzatyoledwa ngati mtengo.

21 Alusira cumba wosabala,

Osamcitira wamasiye cokoma.

22 Mulungu awakhalitsa amphamvu mwa mphamvu yace;

Iwo aukanso m’mene anayesa kuti sadzakhala ndi moyo.

23 Awalola akhale osatekeseka, ndipo alimbikapo;

Koma maso ace ali pa njira zao.

24 Akwezeka; m’kamphindi kuti zi;

Inde atsitsidwa, acotsedwa monga onse ena,

Adutidwa ngati tirigu ngala zace.

25 Ndipo ngati si kutero, anditsutsa ndani kuti ndiri wabodza,

Ndi kuyesa mau anga opanda pace?