Masalmo 2

Ufumu wa wodzozedwa wa Yehova

1 Aphokoseranji amitundu.

Nalingiriranji anthu zopanda pace?

2 Adzikhazikitsa mafumu a dziko lapansi,

Nacita upo akulu pamodzi,

Kutsutsana naye Yehova, ndi Wodzozedwa wace, ndi kuti.

3 Tidule zomangira zao,

Titaye nsinga zao.

4 Wokhala m’mwambayo adzaseka;

Ambuye adzawanyoza.

5 Pomwepo adzalankhula nao mu mkwiyo wace,

Nadzawaopsa m’ukali wace:

6 Koma Ine ndadzoza mfumu yanga

Pa Ziyoni, phiri langa loyera.

7 Ndidzauza za citsimikizo:

Yehova ananena ndi

Ine, Iwe ndiwe Mwana wanga;

Ine lero ndakubala.

8 Undifunse, ndipo ndidzakupatsa amitundu akhale colowa cako,

Ndi malekezero a dziko lapansi akhale ako ako.

9 Udzawatyola ndi ndodo yacitsulo;

Udzawaphwanya monga mbiya yawoumba.

10 Tsono, mafumu inu, citani mwanzeru:

Langikani, oweruza inu a dziko lapansi.

11 Tumikirani Yehova ndi mantha,

Ndipo kondwerani ndi cinthenthe.

12 Mpsompsoneni Mwanayo, kuti angakwiye, ndipo mungatayike m’njira,

Ukayaka pang’ono pokha mkwiyo wace.

Odala onse akumkhulupirira Iye.