Masalmo 3

Kukhulupirika kwa Mulungu

Salimo la Davide, muja anathawa Abisalomu mwana wace.

1 Yehova! Ha! acuruka nanga akundisautsa ine!

Akundiukira ine ndi ambiri.

2 Ambiri amati kwa moyo wanga,

Alibe cipulumutso mwa Mulungu.

3 Ndipo Inu Yehova, ndinu cikopa canga;

Ulemerero wanga, ndi wondiweramutsa mutu wanga.

4 Ndipfuula kwa Yehova ndi mau anga,

Ndipo andiyankha m’phiri lace loyera,

5 Ndinagona ine pansi, ndinagona tulo;

Ndinauka; pakuti Yehova anandicirikiza.

6 Sindidzaopa unyinji wa anthu akundizinga ine.

7 Ukani Yehova; ndipulumutseni, Mulungu wanga!

Pakuti mwapanda adani anga onse patsaya;

Mwawatyola mano oipawo.

8 Cipulumutso nca Yehova;

Dalitso lanu likhale pa anthu anu.