Masalmo 5

Matsoka a oipa, madalitso a olungama

Kwa Mkulu wa Nyimbo; pa Nekiloto. Salimo la Davide.

1 Mverani mau anga, Yehova,

Zindikirani kulingirira kwanga.

2 Tamvetsani mau a kupfuula kwanga,

Mfumu yanga, ndi Mulungu wanga:

Pakuti kwa Inu ndimapemphera,

3 M’mawa, Yehova, mudzamva mau anga;

M’mawa, ndidzakukonzerani pemphero langa, ndipo ndidzadikira.

4 Pakuti Inu sindinu Mulungu wakukondwera naco coipa

Mphulupulu siikhala ndi Inu.

5 Opusa sadzakhazikika pamaso panu:

Mudana nao onse akucita zopanda pace.

6 Mudzaononga iwo akunena bodza:

Munthu wokhetsa mwazi ndi wacinyengo, Yehova anyansidwa naye.

7 Koma ine, mwa kucuruka kwa cifundo canu ndidzalowa m’nyumba yanu:

Ndidzagwada kuyang’ana Kacisi wanu woyera ndi kuopa Inu.

8 Yehova, munditsogolere m’cilungamo canu, cifukwa ca akundizondawo;

Mulungamitse njira yanu pamaso panga.

9 Pakuti m’kamwa mwao mulibe mau okhazikika;

M’kati mwao m’mosakaza;

M’mero mwao ndi manda apululu:

Lilime lao asyasyalika nalo.

10 Muwayese otsutsika Mulungu;

Agwe nao uphungu wao:

M’kucuruka kwa zolakwa zao muwapitikitse;

Pakuti anapikisana ndi Inu.

11 Koma akondwere onse amene athawira kwa Inu,

Apfuule mokondwera kosaleka, popeza muwafungatira;

Nasekere mwa Inu iwo akukonda dzina lanu.

12 Pakuti Inu, Yehova, mudzadalitsa wolungamayo;

Mudzamcinjiriza naco cibvomerezo ngati cikopa.