Masalmo 12

Anthu ndi amabodza, Mulungu ndiye woona

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Seminiti

1 Pulumutsani, Yehova; pakuti wofatsa wasowa;

Pakuti okhulupirika acepa mwa ana a anthu.

2 Amanena za bodza munthu yense ndi mnansi wace:

Amanena ndi mlomo wotyasika, ndi mitima iwiri.

3 Yehova adzadula milomo yonse yotyasika,

Lilime lakudzitamandira:

4 Amene amati, Ndi lilime lathu tidzaposa;

Milomo yathu nja ife eni; mbuye wa pa ife ndani?

5 Cifukwa ca kupasuka kwa ozunzika, cifukwa ca kuusa moyo kwa aumphawi,

Ndiuka tsopano, ati Yehova; Ndidzamlonga mosungika muja alaka-lakamo.

6 Mau a Yehova ndi mau oona;

Ngati siliva woyenga m’ng’anjo yadothi,

Yoiyeretsa kasanu ndi kawiri.

7 Mudzawasunga, Yehova,

Mudzawacinjirizira mbadwo uno ku nthawi zonse.

8 Oipa amayenda mozungulira-zungulira,

Potamanda iwo conyansa mwa ana a anthu.