Masalmo 13

Munkhawa athawira Mulungu namkhulupirira

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salmo la Davide.

1 Mudzandiiwala ciiwalire, Yehova, kufikira liti?

Mudzandibisira ine nkhope yanu kufikira liti?

2 Ndidzacita uphungu m’moyo mwanga kufikira liti,

Pokhala ndi cisoni m’mtima mwanga tsiku lonse?

Adzandiukira ine mdani wanga kufikira liti?

3 Penyani, ndiyankheni, Yehova Mulungu wanga:

Penyetsani maso anga, kuti ndingagone tulo ta imfa;

4 Kuti anganene mdani wanga, Ndamlaka;

Ndipo angakondwere otsutsana nane posunthika ine.

5 Koma ine ndakhulupira pa cifundo canu;

Mtima wanga udzakondwera naco cipulumutso canu:

6 Ndidzayimbira Yehova,

Pakuti anandicitira zokoma.