Masalmo 17

Davide apempha Mulungu amsunge pa ofuna kumuononga

Pemphero la Davide.

1 Yehova, imvani cilungamo, mverani mpfuu wanga;

Cherani khutu ku pemphero langa losaturuka m’milomo ya cinyengo,

2 Pankhope panu paturuke ciweruzo canga;

Maso anu apenyerere zolunjika,

3 Mwayesera mtima wanga; mwandizonda usiku;

Mwandisuntha, simupeza kanthu;

Ndatsimikiza mtima kuti m’kamwa mwanga simudzalakwa.

4 Za macitidwe a anthu, ndaceniera ndi mau a milomo yanu

Ndingalowe njira za woononga.

5 M’mayendedwe anga ndasunga mabande anu,

Mapazi anga sanaterereka.

6 Ine ndinakuitanani, pakuti mudzandiyankha, Mulungu:

Cherani khutu lanu kwa ine, imvani mau anga.

7 Onetsani cifundo canu codabwiza, Inu wakupulumutsa okhulupirira Inu

Kwa iwo akuwaukira ndi dzanja lanu lamanja.

8 Ndisungeni monga kamwana ka m’diso,

Ndifungatireni mu mthunzi wa mapiko anu,

9 Kundilanditsa kwa oipa amene andipasula,

Adani a pa moyo wanga amene andizinga.

10 Mafuta ao awatsekereza;

M’kamwa mwao alankhula modzikuza.

11 Tsopano anatizinga m’mayendedwe athu:

Apenyetsetsa m’maso kuti atigwetse pansi.

12 Afanana ndi mkango wofuna kumwetula,

Ndi msona wa mkango wakukhala mobisalamo.

13 Ukani Yehova,

Mumtsekereze, mumgwetse:

Landitsani moyo wanga kwa woipa ndi lupanga lanu;

14 Kwa anthu, ndi dzanja lanu, Yehova,

Kwa anthu a dziko lapansi pano amene colowa cao ciri m’moyo uno,

Ndipo mimba yao muidzaza ndi cuma canu cobisika:

Akhuta mtima ndi ana,

Nasiyira ana amakanda zocuruka zao.

15 Koma ine ndidzapenyerera nkhope yanu m’cilungamo:

Ndidzakhuta mtima ndi maonekedwe anu, pamene ndidzauka.