Masalmo 19

Davide alemekeza zolengedwa ndi Mulungu, ndi malamulo ao omwe

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salmo la Davide

1 Zakumwamba zimalalikira ulemerero wa Mulungu;

Ndipo thambo lionetsa nchito ya manja ace.

2 Usana ndi usana ucurukitsa mau,

Ndipo usiku ndi usiku uonetsa nzeru.

3 Palibe cilankhulidwe, palibe mau;

Liu lao silimveka.

4 Muyeso wao wapitirira pa dziko lonse lapansi,

Ndipo mau ao ku malekezero a m’dziko muli anthu.

Iye anaika hema la dzuwa m’menemo,

5 Ndipo liri ngati mkwati wakuturuka m’cipinda mwace,

Likondwera ngati ciphona kuthamanga m’njira.

6 Kuturuka kwace lituruka kolekezera thambo,

Ndipo kuzungulira kwace lifikira ku malekezero ace:

Ndipo kulibe kanthu kobisalira kutentha kwace.

7 Malamulo a Yehova ali angwiro, akubwezera moyo;

Mboni za Yehova ziri zokhazikika, zakuwapatsa opusa nzeru;

8 Malangizo a Yehova ali olungama, akukondweretsa mtima:

Malamulo a Yehova ali oyera, akupenyetsa maso.

9 Kuopa Yehova kuli mbe, kwakukhalabe nthawi zonse:

Maweruzo a Yehova ali oona, alungama konse konse.

10 Ndizo zifunika koposa golidi, inde, golidi wambiri woyengetsa:

Zizuna koposa uci ndi zakukha za zisa zace,

11 Ndiponso kapolo wanu acenjezedwa nazo:

M’kuzisunga izo muli mphotho yaikuru.

12 Adziwitsa zolowereza zace ndani?

Mundimasule kwa zolakwa zobisika.

13 Ndiponso muletse kapolo wanu pa zodzitama;

Zisacite ufumu pa ine: pamenepo ndidzakhala wangwiro,

Ndi wosacimwa colakwa cacikuru.

14 Mau a m’kamwa mwanga ndi maganizo a m’mtima wanga abvomerezeke pamaso panu,

Yehova, thanthwe langa, ndi Mombolo wanga,