Masalmo 20

Kupempherera mfumu poturukira iye kunkhondo

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salmo la Davide.

1 Yehova akubvomereze tsiku la nsautso;

Dzina la Mulungu wa Yakobo likuike pamsanje;

2 Likutumizire thandizo loturuka m’malo oyera,

Ndipo likugwirizize kucokera m’Ziyoni;

3 Likumbukile zopereka zako zonse,

Lilandire nsembe yako yopsereza;

4 Likupatse ca mtima wako,

Ndipo likwaniritse upo wako wonse.

5 Tidzapfuula mokondwera mwa cipulumutso canu,

Ndipo m’dzina la Mulungu wathu tidzakweza mbendera:

Yehova akwaniritse mapempho ako onse.

6 Tsopano ndidziwa kuti Yehova apulumutsa wodzozedwa wace;

Adzambvomereza m’Mwamba mwace moyera

Ndi mphamvu ya cipulumutso ca dzanja lace lamanja.

7 Ena atama magareca, ndi ena akavalo:

Koma ife tidzachula dzina la Yehova Mulungu wathu.

8 Iwowa anagonieka, nagwa:

Koma ife tauka, ndipo takhala ciriri.

9 Yehova, pulumutsani,

Mfumuyo atibvomereze tsiku lakuitana ife.