Masalmo 28

Apempha cipulumutso, ayamika populumutsidwa

Salmo la Davide.

1 Kwa Inu, Yehova, ndidzapfuulira;

Thanthwe langa, musandikhalire ngati wosamva:

Pakuti ngati munditontholera ine,

Ndidzafanana nao iwo akutsikira kumanda.

2 Mverani mau a kupemba kwanga, pamene ndilirira Inu,

Pamene ndikweza manja anga kuloza ponenera panu poyera.

3 Musandikoke kundicotsa pamodzi ndi oipa,

Ndi ocita zopanda pace;

Amene alankhula zamtendere ndi anansi ao,

Koma mumtima mwao muli coipa.

4 Muwapatse monga mwa nchito zao, ndi monga mwa coipa cocita iwo:

Muwapatse monga mwa macitidwe a manja ao;

Muwabwezere zoyenera iwo.

5 Pakuti sasamala nchito za Yehova,

Kapena macitidwe a manja ace,

Adzawapasula, osawamanganso.

6 Wodalitsika Yehova,

Pakuti adamva mau a kupemba kwanga.

7 Yehova ndiye mphamvu yanga, ndi cikopa canga;

Mtima wanga wakhulupirira Iye, ndipo anandithandiza:

Cifukwa cace mtima wanga ukondwera kwakukuru;

Ndipo ndidzamyamika nayo Nyimbo yanga.

8 Yehova ndiye mphamvu yao,

Inde mphamvu ya cipulumutso ca wodzozedwa wace.

9 Pulumutsani anthu anu, ndi kudalitsa colandira canu:

Muwawetenso, ndi kuwanyamula nthawi zonse.