Masalmo 33

Alemekeza Mulungu wolenga, wosunga zonse

1 Pfuulani mokondwera mwa Yehova, inu olungama mtima:

Oongoka mtima ayenera kulemekeza.

2 Yamikani Yehova ndi zeze:

Myimbireni ndi cisakasa ca zingwe khumi.

3 Mumyimbire Iye Nyimbo yatsopano;

Muyimbe mwaluso kumveketsa mau.

4 Pakuti mau a Yehova ali olunjika;

Ndi nchito zace zonse zikhulupirika.

5 Iye ndiye wakukonda cilungamo ndi ciweruzo:

Dziko lapansi ladzala ndi cifundo ca Yehova.

6 Zakumwamba zinalengedwa ndi mau a Yehova;

Ndipo ndi mpweya wa m’kamwa mwace khamu lao lonse.

7 Amaunjika madzi a m’nyanja monga mulu:

Amakundika zakudya mosungiramo.

8 Dziko lonse lapansi liope Yehova:

Ponse pali anthu acite mantha cifukwa ca Iye,

9 Pakuti ananena, ndipo cinacitidwa;

Analamulira, ndipo cinakhazikika.

10 Yehova aphwanya upo wa amitundu:

Asandutsa cabe zolingirira za mitundu ya anthu.

11 Ciweruzo ca Yehova cikhazikika cikhazikikire,

Zolingirira za m’mtima mwace ku mibadwo mibadwo.

12 Wodalitsika mtundu wa anthu umene Yehova ndiye Mulungu wao;

Mtundu womwe anausankha ukhale colandira ca iye yekha.

13 Yehova apenyerera m’mwamba; Aona ana onse a anthu.

14 M’malo akhalamo Iye, amapenya pansi

Pa onse akukhala m’dziko lapansi;

15 Iye amene akonza mitima ya iwo onse,

Amene azindikira zocita zao zonse.

16 Palibe mfumu yoti gulu lalikuru limpulumutsa:

Mphamvu yaikuru siicilanditsa ciphona,

17 Kavalo safikana kupulumuka naye:

Cinkana mphamvu yace njaikuru sapulumutsa.

18 Taonani, diso la Yehova liri pa iwo akumuopa Iye,

Pa iwo akuyembekeza cifundo cace;

19 Kupulumutsa moyo wao kwa imfa,

Ndi kuwasunga ndi moyo m’nyengo ya njala.

20 Moyo wathu walindira Yehova:

Iye ndiye thandizo lathu ndi cikopa cathu.

21 Pakuti mtima wathu udzakondwera mwa Iye,

Cifukwa takhulupirira dzina lace loyera.

22 Yehova, cifundo canu cikhale pa ife,

Monga takuyembekezani Inu.