Kuipitsitsa kwa anthu, kukometsetsa kwa Mulungu
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide, mtumiki wa Yehova.
1 Colakwa ca woipayo cimati m’kati mwa mtima wanga,
Palibe kuopa Mulungu pamaso pace.
2 Pakud adzidyoletsa yekha m’kuona kwace,
Kuti anthu sadzacipeza coipa cace ndi kukwiya naco.
3 Mau a pakamwa pace ndiwo opanda pace ndi onyenga:
Waleka kuzindikira ndi kucita bwino.
4 Alingirira zopanda pace pakama pace;
Adziika panjira posad pabwino;
Coipa saipidwa naco.
5 Yehova, m’mwambamuli cifundo canu;
Coonadi canu cifikira kuthambo.
6 Cilungamo canu cikunga mapiri a Mulungu;
Maweruzo anu akunga cozama cacikuru:
Yehova, musunga munthu ndi nyama.
7 Ha! cifundo canu, Mulungu, ncokondedwadi!
Ndipo ana a anthu athawira ku mthunzi wa mapiko anu.
8 Adzakhuta kwambiri ndi zonona za m’nyumba mwanu:
Ndipo mudzawamwetsa mu mtsinje wa zokondweretsa zanu.
9 Pakuti citsime ca moyo ciri ndi Inu:
M’kuunika kwanu tidzaona kuunika.
10 Tanimphitsani cifundo canu pa iwo akudziwa Inu;
Ndi cilungamo canu pa oongoka mtima.
11 Phazi la akudzikuza lisandifikire ine,
Ndi dzanja la oipa lisandicotse.
12 Pomwepo padagwera ocita zopanda pace:
Anawalikha, ndipo sadzatha kuukanso.