Masalmo 39

Kupepuka kwa moyo uno

Kwa Mkulu wa Nyimbo, kwa Yedutun, Salmo la Davide.

1 Ndinati, Ndidzasunga njira zanga,

Kuti ndingacimwe ndi lilime langa:

Ndidzasunga pakamwa panga ndi cam’kamwa,

Pokhala woipa ali pamaso panga.

2 Ndinatonthola osanena mau, ndinakhala cete osalawa cokoma;

Ndipo cisoni canga cinabuka.

3 Mtima wanga unatentha m’kati mwaine;

Unayaka moto pakulingirira ine:

Pamenepo ndinalankhula ndi lilime langa:

4 Yehova, mundidziwitse cimariziro canga,

Ndi mawerengedwe a masiku anga ndi angati;

Ndidziwe malekezero anga,

5 Onani, munaika masiku anga akhale monga kuyesa dzanja;

Ndipo zaka zanga ziri ngati cabe pamaso panu:

Indedi munthu ali yense angakhale wokhazikika, ali cabe konse.

6 Indedi munthu ayenda ngati mthunzi:

Indedi abvutika cabe:

Asonkhanitsa cuma, ndipo sadziwa adzacilandira ndani?

7 Ndipo tsopano, Ambuye, ndilindira ciani?

Ciyembekezo canga ciri pa Inu.

8 Ndipulumutseni kwa zolakwa zangazonse:

Musandiike ndikhale cotonza ca wopusa.

9 Ndinakhala du, sindinatsegula pakamwa panga;

Cifukwa inu mudacicita.

10 Mundicotsere cobvutitsa canu;

Pandithera ine cifukwa ca kulanga kwa dzanja lanu.

11 Pamene mulanga munthu ndi zomdzudzula cifukwa ca mphulupulu,

Mukanganula kukongola kwace monga mumacita ndi kadzoce:

Indedi, munthu ali yense ali cabe.

12 Imvani pemphero langa, Yehova, ndipo cherani khutu kulira kwanga;

Musakhale cete pa misozi yanga:

Pakuti ine ndine mlendo ndi Inu,

Wosakhazikika, monga makolo anga onse.

13 Ndiloleni, kuti nditsitsimuke,

Ndisanamuke ndi kukhala kuli zi.