Masalmo 40

Alemekeza cipulumutso ca Mulungu, alalikira poyera cilungamo ca Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salmo la Davide.

1 Kuyembekeza ndayembekeza Yehova;

Ndipo anandilola, namva kupfuula kwanga.

2 Ndipo anandikweza kunditurutsa m’dzenje la citayiko, ndi m’thope la pacithaphwi;

Nandipondetsa pathanthwe, nakhazika mayendedwe anga.

3 Ndipo anapatsa Nyimbo yatsopano m’kamwa mwanga, cilemekezo ca kwa Mulungu wanga;

Ambiri adzaciona, nadzaopa,

Ndipo adzakhulupirira Yehova.

4 Wodala munthuyo wakuyesa Yehova wokhulupirika;

Wosasamala odzikuza, ndi opatukira kubodza.

5 Inu, Yehova, Mulungu wanga, zodabwiza zanu mudazicita nzambiri,

Ndipo zolingirira zanu za pa ife;

Palibe wina wozifotokozera Inu;

Ndikazisimba ndi kuzichula, Zindicurukira kuziwerenga.

6 Nsembe ndi copereka simukondwera nazo;

Mwanditsegula makutu:

Nsembe yopsereza ndi yamacimo simunapempha.

7 Pamenepo ndinati, Taonani, ndadza;

M’buku mwalembedwa za Ine:

8 Kucita cikondwero canu kundikonda, Mulungu wanga;

Ndipo malamulo anu ali m’kati mwamtima mwanga.

9 Ndalalikira cilungamo mu msonkano waukuru;

Onani, sindidzaletsa milomo yanga,

Mudziwa ndinu Yehova.

10 Cilungamo canu sindinacibisa m’kati mwamtima mwanga;

Cikhulupiriko canu ndi cipulumutso canu ndinacinena;

Cifundo canu ndi coonadi canu sindinacibisira msonkhano waukuru.

11 Inu Yehova, simudzandikaniza nsoni zanu:

Cifundo canu ndi coonadi canu zindisunge cisungire.

12 Pakuti zoipa zosawerengeka zandizinga,

Zocimwa zanga zandipeza kotero kuti sindikhoza kupenya;

Ziposa tsitsi la mutu wanga, ndipo wandicokera mtima.

13 Ndikupemphani, Yehova, ndilanditseni:

Fulumirani kudzandithandiza, Yehova.

14 Acite manyazi nadodome

Iwo akulondola moyo wanga kuti auononge:

Abwerere m’mbuyo, nacite manyazi iwo okondwera kundicitira coipa.

15 Apululuke, mobwezera manyazi ao

Amene anena nane, Hede, hede.

16 Asekerere nakondwerere mwa Inu onse akufuna Inu:

Iwo akukonda cipulumutso canu asaleke kunena, Abuke Yehova.

17 Ndipo ine ndine wozunzika ndi waumphawi;

Koma Ambuye andikumbukila ine:

Inu ndinu mthandizi wanga, ndi mpulumutsi wanga:

Musamacedwa, Mulungu wanga,