Davide alira akhale ku Kacisi
1 Mundiweruzire, Mulungu, ndipo mundinenere mlandu kwa anthu opanda cifundo:
Mundilanditse kwa munthu wonyenga ndi wosalungama.
2 Pakuti Inu ndinu Mulungu wa mphamvu yanga; mwanditayiranji?
Ndimayenderanji woliralira cifukwa ca kundipsinja mdani?
3 Tumizirani kuunika kwanu ndi coonadi canu zinditsogolere:
Zindifikitse ku phiri lanu loyera,
Kumene mukhala Inuko.
4 Kuti ndipite kufikira guwa la nsembe la Mulungu,
Kufikira Mulungu wa cimwemwe canga ceniceni:
Ndi kuti ndikuyamikeni ndi zeze, Mulungu, Mulungu wanga.
5 Udziweramiranji moyo wanga iwe?
Ndi kuzingwa m’kati mwanga?
Yembekeza Mulungu: pakuti ndidzamyamikanso,
Ndiye cipulumutso ca nkhope yanga, ndi Mulungu wanga.