Masalmo 46

Mulungu ndiye pothawirapo anthu ace

Kwa Mkulu wa Nyimbo; Cilangizo ca kwa ana a Kora. Pa Alamot. Nyimbo.

1 Mulungu ndiye pothawirapo pathu ndi mphamvu yathu,

Thandizo lopezekeratu m’masautso.

2 Cifukwa cace sitidzacita mantha, lingakhale lisandulika dziko lapansi,

Angakhale mapiri asunthika, nakhala m’kati mwa nyanja;

3 Cinkana madzi ace akokoma, nacita thobvu,

Nagwedezeka mapiri ndi kudzala kwace.

4 Pali mtsinje, ngalande zace zidzakondweretsa mudzi wa Mulungu.

Malo oyera okhalamo Wam’mwambamwamba,

5 Mulungu ali m’kati mwace, sudzasunthika:

Mulungu adzauthandiza mbanda kuca.

6 Amitundu anapokosera; maufumu anagwedezeka:

Ananena mau, dziko lapansi linasungunuka.

7 Yehova wa makamu ali ndi ife;

Mulungu wa Yakobo ndiye pamsanje pathu.

8 Idzani, penyani nchito za Yehova,

Amene acita zopululutsa pa dziko lapansi.

9 Aletsa nkhondo ku malekezero adziko lapansi;

Athyola uta, nadula nthungo;

Atentha magareta ndi moto.

10 Khalani cete, ndipo dziwani kuti Ine ndine Mulungu:

Ndidzabuka mwa amitundu,

Ndidzabuka pa dziko lapansi.

11 Yehova wa makamu ali ndi ife,

Mulungu wa Yakobo ndiye pamsanje pathu,