Masalmo 52

Davide aneneratu za cionongeko ca oipa, iye nakhulupirira Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Cilangizo ca Davide. Muja analowa Doegi M-edomu nauza Sauli, nati kwa iye, Davide walowa m’nyumba ya Abimeleke.

1 Udzitamandiranji ndi coipa, ciphonaiwe?

Cifundo ca Mulungu cikhala tsiku lonse.

2 Lilime lako likupanga zoipa;

Likunga lumo lakuthwa, lakucita monyenga.

3 Ukonda coipa koposa cokoma;

Ndi bodza koposa kunena cilungamo.

4 Ukonda mau onse akuononga, Lilime lacinyengo, iwe.

5 Potero Mulungu adzakupasula ku nthawi zonse,

Adzakucotsa nadzakukwatula m’hema mwako,

Nadzakuzula, kukucotsa m’dziko la amoyo.

6 Ndipo olungama adzaciona, nadzaopa,

Nadzamseka, ndi kuti,

7 Tapenyani, suyu munthuyu amene sanamuyesa Mulungu mphamvu yace;

Amene anatama kucuruka kwa cuma cace,

Nadzilimbitsa m’kuipsa kwace.

8 Koma ine ndine ngati mtengo wauwisi waazitona m’nyumba ya Mulungu:

Ndikhulupirira cifundo ca Mulungu ku nthawi za nthawi.

9 Ndidzakuyamikani kosatha, popeza Inu munacicita ici:

Ndipo ndidzayembekeza dzina lanu, pakuti ici ncokoma, pamaso pa okondedwa anu,