Mtima woliralira kuyanfana ndi Mulungu
Salmo la Davide; muja akakhala m’cipululu ca Yuda.
1 Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga; ndidzakufunani m’matanda kuca:
Moyo wanga ukumva ludzu la kwa Inu, thupi langa lilirira Inu,
M’dziko louma ndi lotopetsa, lopanda madzi.
2 Kuti ndione mphamvu yanu ndi ulemerero wanu,
Monga ndinakuonani m’malo oyera.
3 Pakuti cifundo canu ciposa moyo makomedwe ace;
Milomo yanga idzakulemekezani.
4 Potero ndidzakuyamikani m’moyo mwanga;
Ndidzakweza manja anga m’dzina lanu.
5 Mudzakhutitsa moyo wanga ngati ndi mafuta ndi zonona;
Ndipo pakamwa panga ndidzakulemekezani ndi milomo yakupfuula mokondwera;
6 Pokumbukira Inu pa kama wanga,
Ndi kulingalira za Inu maulonda a usiku.
7 Pakuti munakhala mthandizi wanga;
Ndipo ndidzapfuula mokondwera mu mthunzi wa mapiko anu.
8 Moyo wanga uumirira Inu:
Dzanja lamanja lanu lindigwiriziza.
9 Koma iwo amene afuna moyo wanga kuti auononge,
Adzalowa m’munsi mwace mwa dziko.
10 Adzawapereka ku mphamvu ya lupanga;
Iwo adzakhala gawo la ankhandwe.
11 Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu;
Yense wakulumbirira iye adzatamandira;
Pakuti pakamwa pa iwo onena bodza padzatsekedwa.