Masalmo 64

Davide apempha Mulungu amciniirize pa omlalira

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salmo la Davido.

1 Imvani Yehova, mau anga, m’kudandaula kwanga;

Sungani moyo wanga angandiopse mdani.

2 Ndibiseni pa upo wacinsinsi wa ocita zoipa;

Pa phokoso la ocita zopanda pace:

3 Amene anola lilime lao ngati lupanga,

Napiringidza mibvi yao, ndiyo mau akuwawitsa;

4 Kuponyera wangwiro mobisika:

Amponyera modzidzimutsa, osaopa.

5 Alimbikitsana m’cinthu coipa;

Apangana za kuchera misampha mobisika;

Akuti, Adzaiona ndani?

6 Afunafuna zosalungama; kusanthula, asanthuladi kutha;

Cingakhale ca m’kati mwace mwa munthu, ndi mtima wozama.

7 Koma Mulungu adzawaponyera mubvi;

Adzalaswa modzidzimutsa,

8 Adzawakhumudwitsa, lilime lao lidzawatsutsa;

Onse akuwaona adzawathawa.

9 Ndipo anthu onse adzacita mantha;

Nadzabukitsa cocita Mulungu,

Nadzasamalira nchito yace.

10 Wolungama adzakondwera mwa Yehova, nadzakhulupirira Iye;

Ndipo oongoka mtima onse adzalemekeza.