Masalmo 65

Davide alemekeza Mulungu pa madalitso ocuruka

Kwa Mkulu wa Nyimbo; Salimo, nyimbo ya Davide.

1 M’Ziyoni akulemekezani Inu mwacete, Mulungu:

Adzakucitirani Inu cowindaci.

2 Wakumva pemphero Inu,

Zamoyo zonse zidzadza kwa Inu.

3 Mphulupulu zinandilaka;

Koma mudzafafaniza zolakwa zathu.

4 Wodala munthuyo mumsankha, ndi kumyandikizitsa,

Akhale m’mabwalo anu:

Tidzakhuta nazo zokoma za m’nyumba yanu,

Za m’malo oyera a Kacisi wanu.

5 Mudzatiyankha nazo zoopsa m’cilungamo,

Mulungu wa cipulumutso cathu;

Ndinu cikhulupiriko ca malekezero Onse a dziko lapansi,

Ndi ca iwo okhala kutali kunyanja:

6 Ndinu amene mukhazikitsa mapiri ndi mphamvu yanu;

Pozingidwa naco cilimbiko.

7 Amene atontholetsa kukuntha kwa nyanja, kukuntha kwa mafunde ace,

Ndi phokoso la mitundu ya anthu.

8 Ndipo iwo akukhala kumalekezero adzacita mantha cifukwa ca zizindikilo zanu; Mukondweretsa apo paturukira dzuwa, ndi apo lilowera.

9 Muceza nalo dziko lapansi, muhthirira,

Mulilemeza kwambiri;

Mtsinje wa Mulungu udzala nao madzi:

Muwameretsera tirigu m’mene munakonzera nthaka.

10 Mukhutitsa nthaka yace yolima;

Mufafaniza nthumbira zace?

Muiolowetsa ndi mbvumbi;

Mudalitsa mmera wace.

11 Mubveka cakaci ndi ukoma wanu;

Ndipo mabande anu akukha zakuca.

12 Akukha pa mabusa a m’cipululu;

Ndipo mapiri azingika naco cimwemwe.

13 Podyetsa mpodzaza ndi zoweta;

Ndipo zigwa zakutidwa ndi tirigu;

Zipfuula mokondwera, inde ziyimbira.