Masalmo 67

Amitundu alemekeze Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo, pa Neginolo. Salmo, Nyimbo.

1 Aticitire cifundo Mulungu, ndi kutidalitsa,

Atiwalitsire nkhope yace;

2 Kuti njira yanu idziwike pa dziko lapansi,

Cipulumutso canu mwa amitundu onse.

3 Anthu akuyamikeni, Mulungu;

Anthu onse akuyamikeni.

4 Anthu akondwere, napfuule makondwera;

Pakuti mudzaweruza anthu malunjika,

Ndipo mudzalangiza anthu pa dziko lapansi.

5 Anthu akuyamikeni, Mulungu;

Anthu onse akuyamikeni.

6 Dziko lapansi lapereka zipatso zace:

Mulungu, Mulungu wathu adzatidalitsa.

7 Mulungu adzatidalitsa;

Ndipo malekezero onse a dziko lapansi adzamuopa Iye,