Masalmo 70

Davide apempha Mulungu amlanditse msanga

Kwa Mkulu wa Nyimbo: cikumbutso ca Davtde,

1 Fulumirani kundipulumutsa, Mulungu;

Fulumirani kundithandiza, Yehova.

2 Acite manyazi, nadodome

Amene afuna moyo wanga:

Abwezedwe m’mbuyo, napepulidwe.

Amene akonda kundicitira coipa,

3 Abwerere, kukhale mphotho ya manyazi ao

Amene akuti, Hede, hede.

4 Asekerere nakondwerere mwa Inu onse akufuna Inu;

Nanene kosalekeza iwo akukonda cipulumutso canu,

Abuke Mulungu.

5 Koma ine ndine wozunzika ndi waumphawi;

Mundifulumirire, Mulungu:

Inu ndinu mthandizi wanga ndi mpulumutsi wanga;

Musacedwe, Yehova.