Masalmo 76

Ulemerero ndi mphamvu ya Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Negtnolo. Salmo la Asafu. Nyimbo.

1 Mulungu adziwika mwa Yuda:

Dzina lace limveka mwa Israyeli.

2 Msasa wace unali m’Salemu, Ndipo pokhala Iye m’Ziyoni.

3 Pomwepo anatyola mibvi ya paota;

Cikopa, ndi lupanga, ndi nkhondo.

4 Inu ndinu wakuunikira, ndi womveka wakuposa mapiri muli acifwamba.

5 Olimba mtima cifunkhidwa cuma cao, agona tulo tao;

Amuna onse amphamvu asowa manja ao.

6 Pa kudzudzula kwanu, Mulungu wa Yakobo,

Gareta ndi kavalo yemwe anagwa m’tulo.

7 Inu ndinu woopsa;

Ndipo utauka mkwiyo wanu adzakhala ciriri ndani pamaso panu?

8 Mudamveketsa ciweruzo cocokera Kumwamba;

Dziko lapansi linacita mantha, nilinakhala cete,

9 Pakuuka Mulungu kuti aweruze,

Kuti apulumutse ofatsa onse a pa dziko lapansi.

10 Indedi, kuzaza kwace kwa munthu kudzakulemekezani;

Cotsalira ca kuzazaku mudzaciletsa.

11 Windani ndipo citirani Yehova Mulungu wanu zowindazo;

Onse akumzinga abwere naco copereka ca kwa Iye amene ayenera kumuopa.

12 Iye adzadula mzimu wa akulu;

Akhala woopsa kwa mafumu a pa dziko lapansi.