Masalmo 82

Oweruza aweruze bwino

Salmo la Asatu.

1 Mulungu aima mu msonkhano wa Mulungu,

Aweruza pakati pa milungu.

2 Mudzaweruza mosalunjika kufikira liti,

Ndi kusamalira nkhope ya oipa?

3 Weruzani osauka ndi amasiye;

Weruzani molungama ozunzika ndi osowa.

4 Pulumutsani osauka ndi aumphawi:

Alanditseni m’dzanja la oipa,

5 Sadziwa, ndipo sazindikira;

Amayendayenda mumdima;

Maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

6 Ndinati Ine, Inu ndinu milungu,

Ndi ana a Wam’mwambamwamba nonsenu.

7 Komatu mudzafa monga anthu,

Ndipo mudzagwa monga wina wa akulu.

8 Ukani, Mulungu, weruzani dziko lapansi;

Pakuti Inu mudzalandira amitundu onse.