Masalmo 83

Amitundu apangana kuononga Aisrayeli, Apempha Mulungu awalanditse

Nyimbo. Satmo la Asatu.

1 Mulungu musakhale cete;

Musakhale du, osanena kanthu, Mulungu.

2 Pakuti taonani, adani anu aphokosera:

Ndipo okwiyira Inu aweramutsa mutu,

3 Apangana mocenjerera pa anthu anu,

Nakhalira upo pa obisika anu.

4 Amati, Tiyeni tiwaononge asakhalenso mtundu wa anthu;

Ndipo dzina la Israyeli lisakumbukikenso.

5 Pakuti anakhalira upo ndi mtima umodzi;

Anacita cipangano ca pa Inu:

6 Mahema a Edomu ndi a Aismayeli;

Moabu ndi Ahagara;

7 Gebala ndi Amoni ndi Amaleki;

Filistiya, pamodzi ndi iwo okhala m’Turo.

8 Asuri anaphatikana nao;

Anakhala dzanja la ana a Loti,

9 Muwacitire monga munacitira Midyani;

Ndi Sisera, ndi Jabini ku mtsinje wa Kisoni:

10 Amene anaonongeka ku Endoro;

Anakhala ngati ndowe ya kumunda.

11 Muwaike akulu ao ngati Orebu ndi Zeebu;

Mafumu ao ngati Zeba ndi Zalimuna:

12 Amene anati, Tilande

Malo okhalamo Mulungu, akhale athu.

13 Mulungu wanga, muwaike akhale ngati mungu;

Ngati ziputu zomka ndi mphepo.

14 Monga moto upsereza nkhalango,

Ndi monga lawi liyatsa mapiri;

15 Momwemo muwatsate ndi namondwe,

Nimuwaopse ndi kabvumvulu wanu.

16 Acititseni manyazi pankhope pao;

Kuti afune dzina lanu, Yehova.

17 Acite manyazi, naopsedwe kosatha;

Ndipo asokonezeke, naonongeke:

18 Kuti adziwe kuti inu nokha, dzina lanu ndinu Yehova,

Ndinu Wam’mwambamwamba pa dziko lonse lapansi.