Masalmo 92

Anthu onse ayamike Mulungu cifukwa ca nchito zace, cilungamo cace, ndi cifundo cace

Satmo, Nyimbo ya pa Sabata,

1 Nkokoma kuyamika Yehova,

Ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Wam’mwambamwamba Inu:

2 Kuonetsera cifundo canu mamawa,

Ndi cikhulupiriko canu usiku uli wonse.

3 Pa coyimbira ca zingwe khumi ndi pacisakasa;

Pazeze ndi kulira kwace.

4 Popeza Inu, Yehova, munandikondweretsa ndi kucita kwanu,

Ndidzapfuula mokondwera pa nchito ya manja anu.

5 Ha! nchito zanu nzazikuru, Yehova,

Zolingalira zanu nzozama ndithu.

6 Munthu wopulukira sacidziwa;

Ndi munthu wopusa sacizindikira ici;

7 Cakuti pophuka oipa ngati msipu,

Ndi popindula ocita zopanda pace;

Citero kuti adzaonongeke kosatha:

8 Koma Inu, Yehova, muli m’mwamba ku nthawi yonse.

9 Pakuti, taonani, adani anu, Yehova,

Pakuti, taonani, adani anu adzatayika;

Ocita zopanda pace onse adzamwazika.

10 Koma munakweza nyanga yanga ngati ya njati;

Anandidzoza mafuta atsopano.

11 Diso langa lapenya cokhumba ine pa iwo ondilalira,

M’makutu mwanga ndamva cokhumba ine pa iwo akucita zoipa akundiukira.

12 Wolungama adzaphuka ngati mgwalangwa;

Adzakula ngati mkungudza wa ku Lebano.

13 Iwo ookedwa m’nyumba ya Yehova,

Adzaphuka m’mabwalo a Mulungu wathu.

14 Atakalamba adzapatsanso zipatso;

Adzadzazidwa ndi madzi nadzakhala abiriwiri:

15 Kulalikira kuti Yehova ngwolunjika;

Iye ndiye thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe cosalungama.