Ufumu wa Mulungu ndiwo wa ulemerero, mphamvu, ndi ciyero
1 Yehova acita ufumu; wadzibveka ndi ukulu;
Wadzibveka Yehova, wadzimangirira mphamvu m’cuuno;
Dziko lomwe lokhalamo anthu likhazikika, silidzagwedezeka.
2 Mpando wacifumu wanu ukhazikika kuyambira kale lija;
Inu ndinu wosayambira ndi kale, lomwe.
3 Mitsinje ikweza, Yehova,
Mitsinje ikweza mkokomo wao;
Mitsinje ikweza mafunde ao.
4 Yehova Wam’mwamba ndiye wamphamvu,
Wakuposa mkokomo wa madzi ambiri,
Ndi mafunde olimba a nyanja.
5 Mboni zanu zibvomerezeka ndithu;
Ciyero ciyenera nyumba yanu, Yehova, ku nthawi za muyaya.