Masalmo 96

Onse a pansi pano ndi am’mwamba omwe alemekeze Mulungu

1 Myimbireni Yehova nyimbo yatsopano;

Myimbireni Yehova, inu, dziko lonse lapansi.

2 Myimbireni Yehova, lemekezani dzina lace;

Lalikirani cipulumutso cace tsiku ndi tsiku.

3 Fotokozerani ulemerero wace mwa amitundu;

Zodabwiza zace mwa mitundu yonse ya anthu.

4 Pakuti Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu;

Ayenera amuope koposa milungu yonse.

5 Pakuti milungu yonse ya mitundu ya anthu ndiyo mafano:

Koma Yehova analenga zakumwamba.

6 Pamaso pace pali ulemu ndi ukulu:

M’malo opatulika mwace muli mphamvu ndi zocititsa kaso.

7 Mpatseni Yehova, inu, mafuko a mitundu ya anthu,

Mpatseni Yehova ulemerero ndi mphamvu,

8 Mpatseni Yehova ulemerero wa dzina lace;

Bwerani naco copereka, ndipo fikani ku mabwalo ace.

9 Gwadirani Yehova moyera ndi mokometsetsa:

Njenjemerani pamaso pace, inu dziko lonse lapansi.

10 Nenani mwa amitundu, Yehova acita ufumu;

Dziko lokhalamo anthu lomwe likhazikika kuti silingagwedezeke;

Adzaweruza mitundu ya anthu molunjika.

11 Kumwamba kukondwere nilisekerere dziko lapansi;

Nyanja ibume mwa kudzala kwace:

12 Munda ukondwerere ndi zonse ziri m’mwemo;

Pamenepo mitengo yonse ya kunkhalango idzapfuula mokondwera;

13 Pamaso pa Yehova, pakuti akudza;

Pakuti akudza kudzaweruza dziko lapansi:

Adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi cilungamo,

Ndi mitundu ya anthu ndi coonadi.