Masalmo 97

Ulemerero wa ufumu wa Mulungu

1 Yehova acita ufumu; dziko lapansi likondwere;

Zisumbu zambiri zikondwerere.

2 Pomzinga pali mitambo ndi mdima;

Cilungamo ndi ciweruzo ndizo zolimbitsa mpando wacifumu wace.

3 Moto umtsogolera,

Nupsereza otsutsana naye pozungulirapo,

4 Mphezi zace zinaunikira dziko lokhalamo anthu;

Dziko lapansi linaona nilinagwedezeka.

5 Mapiri anasungunuka ngati sera pamaso pa Yehova,

Pamaso pa Ambuye wa dziko lonse lapansi.

6 Kumwamba kulalikira cilungamo cace,

Ndipo mitundu yonse ya anthu ipenya ulemerero wace.

7 Onse akutumikira fano losema,

Akudzitamandira nao mafano, acite manyazi:

Mgwadireni Iye, milungu yonse inu.

8 Ziyoni anamva nakondwera,

Nasekerera ana akazi a Yuda;

Cifukwa ca maweruzo anu, Yehova.

9 Pakuti Inu, Yehova, ndinu Wam’mwambamwamba pa dziko lonse lapansi,

Ndinu wokwezeka kwakukuru pamwamba pa milungu yonse yina.

10 Inuokonda Yehova, danani naco coipa:

Iye asunga moyo wa okondedwa ace;

Awalanditsa m’manja mwa oipa.

11 Kuunika kufesekera wolungama, Ndi cikondwerero oongoka mtima.

12 Kondwerani mwa Yehova, olungama inu;

Ndipo yamikani pokumbukila ciyero cace.