Alemekeze Mulungu pa cifundo ndi coonadi cao
Sa1mo.
1 Myimbireni Yehova nyimbo yatsopano;
Popeza anacita zodabwiza:
Dzanja lace lamanja, mkono wace woyera, zinamcitira cipulumutso,
2 Yehova anawadziwitsira cipulumutso cace;
Anaonetsera cilungamo cace pamaso pa amitundu.
3 Anakumbukila cifundo cace ndi cikhulupiriko cace ku nyumba ya Israyeli;
Malekezero onse a dziko lapansi anaona cipulumutso ca Mulungu wathu.
4 Pfuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi;
Kuwitsani ndi kupfuulira mokondwera; inde, yimbirani zomlemekeza.
5 Myimbireni Yehova zomlemekeza ndizeze;
Ndi zeze ndi mau a salmo.
6 Pfuulani pamaso pa Mfumu Yehova,
Ndi mbetete ndi liu la lipenga,
7 Nyanja Ipfuule ndi kudzala kwace;
Dziko lokhalamo anthu ndi iwo okhalamo;
8 Mitsinje iombe manja;
Mapiri apfuule pamodzi mokondwera;
9 Pamaso pa Yehova, popeza akudza kudzaweruza dziko lapansi;
Adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi cilungamo,
Ndi mitundu ya anthu molunjika,