Masalmo 99

Mulungu wamkuru wacifundo alemekezedwe

1 Yehova ndiye mfumu; mitundu ya anthu injenjemere;

Iye akhala pakati pa akerubi; dziko lapansi ligwedezeke.

2 Yehova ndiye wamkuru m’Ziyoni;

Ndipo akwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.

3 Alemekeze dzina lanu lalikuru ndi loopsa;

Ili ndilo loyera.

4 Ndipo mphamvu ya mfumu ikonda ciweruzo;

Inu mukhazikitsa zolunjika,

Mucita ciweruzo ndi cilungamo m’Yakobo.

5 Mkwezeni Yehova Mulungu wathu,

Ndipo padirani poponderapo mapasa ace:

Iye ndiye Woyera.

6 Mwa ansembe ace muli Mose ndi Aroni,

Ndi Samueli mwa iwo akuitanira dzina lace;

Anaitana kwa Yehova, ndipo Iye anawayankha.

7 Iye analankhula nao mumtambo woti njo:

Iwo anasunga mboni zace ndi malembawa anawapatsa,

8 Munawayankha, Yehova Mulungu wathu:

Munawakhalira Mulungu wakuwakhululukira,

Mungakhale munabwezera cilango pa zocita zao.

9 Mkwezeni Yehova Mulungu wathu,

Ndipo gwadirani pa phiri lace loyera;

Pakuti Yehova Mulungu wathu ndiye woyera.