Olengedwa ndi Mulungu amlemekeze
Salmo la Ciyamiko.
1 Pfuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi.
2 Tumikirani Yehova ndi cikondwerero:
Idzani pamaso pace ndi kumyimbira mokondwera,
3 Dziwani kuti Yehova ndiye Mulungu;
Iyeyu anatilenga, ndipo ife ndife ace;
Ndife anthu ace ndi nkhosa za pabusa pace.
4 Lowani ku zipata zace ndi ciyamiko,
Ndi ku mabwalo ace ndi cilemekezo:
Myamikeni; lilemekezeni dzina lace.
5 Pakuti Yehova ndiye wabwino; cifundo cace cimamka muyaya;
Ndi cikhulupiriko cace ku mibadwo mibadwo.