Wa Salmo alemekeza Mulungu womlanditsa m’manja mwa adani
1 Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino;
Pakuti cifundo cace ncosatha.
2 Anene tsono Israyeli,
Kuti cifundo cace ncosatha.
3 Anene tsono nyumba ya Aroni,
Kuti cifundo cace ncosatha.
4 Anene tsono iwo akuopa Yehova,
Kuti cifundo cace ncosatha.
5 M’mene ndinasautsika ndinaitanira pa Yehova;
Anandiyankha Dandiika motakasuka Yehova.
6 Yehova ndi wanga; sindidzaopa;
Adzandicitanji munthu?
7 Yehova ndi wanga, mwa iwo akundithandiza;
M’mwemo ndidzaona cofuna ine pa iwo akundida,
8 Kuthawira kwa Yehova nkokoma
Koposa kukhulupirira munthu.
9 Kuthawira kwa Yehova nkokoma
Koposa kukhulupirira akulu,
10 Amitundu onse adandizinga,
Zedi, m’dzina la Yehova ndidzawaduladula.
11 Adandizinga, inde, adandizinga:
Indedi, m’dzinala Yehova ndidzawaduladula.
12 Adandizinga ngati njuci;
Anazima ngati moto waminga;
Indedi, m’dzina la Yehova ndidzawaduladula.
13 Kundikankha anandikankha ndikadagwa;
Koma Yehova anandithandiza.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;
Ndipo anakhala cipulumutso canga.
15 M’mahema a olungama muli liu lakupfuula mokondwera ndi la cipulumutso:
16 Dzanja lamanja la Yehova licita mwamphamvu.
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo,
Ndipo ndidzafotokozera nchito za Yehova.
18 Kulanga anandilangadi Yehova:
Koma sanandipereka kuimfa ai.
19 Nditsegulireni zipata za cilungamo;
Ndidzalowamo, ndidzayamika Yehova.
20 Cipata ca Yehova ndi ici;
Olungama adzalowamo.
21 Ndidzakuyamikani, popeza munandiyankha,
Ndipo munakhala cipulumutso canga,
22 Mwala umene omangawo anaukana
Wakhala mutu wa pangondya.
23 Ici cidzera kwa Yehova;
Ncodabwiza ici pamaso pathu.
24 Tsiku ili ndilo adaliika Yehova;
Tidzasekera ndi kukondwera m’mwemo.
25 Tikupemphani, Yehova, tipulumutseni tsopano;
Tikupemphani, Yehova, tipindulitseni tsopano.
26 Wodala wakudzayo m’dzina la Yehova;
Takudalitsani kocokera m’nyumba ya Yehova.
27 Yehova ndiye Mulungu, amene anatiunikira;
Mangani nsembe ndi zingwe, ku nyanga za guwa la nsembe.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani;
Ndinu Mulungu wanga, ndidzakukwezani.
29 Yamikani Yehova, pakuti Iye ndiye wabwino,
Pakuti cifundo cace ncosatha.