Masalmo 120

Apempha Mulungu amlanditse pa Omnamiza

Nyimbo yokwerera.

1 Ndinapfuulira kwa Yehova mu msauko wanga,

Ndipo anandibvomereza,

2 Yehova, landitsani moyo wanga ku milomo ya mabodza,

Ndi ku lilime lonyenga.

3 Adzakuninkhanji, adzakuonjezeranji,

Lilime lonyenga iwe?

4 Mibvi yakuthwa ya ciphona.

Ndi makara tsanya.

5 Tsoka ine, kuti ndiri mlendo m’Meseke,

Kuti ndigonera m’mahema a Kedara!

6 Moyo wanga unakhalitsa nthawi

Pamodzi ndi iye wakudana nao mtendere.

7 Ine ndikuti, Mtendere;

Koma polankhula ine, iwowa akuti, Nkhondo.