Masalmo 122

Apempherera mtendere wa Yerusalemu

Nyimbo yokwerera: ya Davide.

1 Ndinakondwera m’mene ananena nane,

Tiyeni ku nyumba ya Yehova.

2 Mapazi athu alinkuima M’zipata zanu, Yerusalemu.

3 Yerusalemu anamangidwa

Ngati mudzi woundana bwino:

4 Kumene akwerako mafuko, ndiwo mafuko a Yehova;

Akhale mboni ya kwa Israyeli,

Ayamike dzina la Yehova.

5 Pakuti pamenepo anaika mipando ya ciweruzo,

Mipando ya nyumba ya Davide.

6 Mupempherere mtendere wa Yerusalemu;

Akukonda inu adzaona phindu.

7 M’linga mwako mukhale mtendere,

M’nyumba za mafumu mukhale phindu.

8 Cifukwa ca abale anga ndi mabwenzi anga,

Ndidzanena tsopano, Mukhale mtendere mwa inu.

9 Cifukwa ca nyumba ya Yehova Mulungu wathu

Ndidzakufunira zokoma,