Masalmo 123

Pemphero la wonyozedwa

Nyimbo yokwerera.

1 Ndikweza maso anga kwa Inu,

Kwa Inu wakukhala kumwamba.

2 Taonani, monga maso a anyamata ayang’anira dzanja la ambuye ao,

Monga maso a adzakazi ayang’anira dzanja la mbuye wao wamkazi:

Momwemo maso athu ayang’anira Yehova Mulungu wathu,

Kufikira aticitira cifundo.

3 Muticitire cifundo, Yehova, muticitire cifundo;

Pakuti takhuta kwambiri ndi mnyozo.

4 Moyo wathu wakhuta ndithu

Ndi kuseka kwa iwo osasowa kanthu,

Ndi mnyozo wa odzikuza.