Masalmo 124

Mulungu yekha walanditsa anthu ace

Nyimbo vokwerera: ya Davide,

1 Akadapanda kukhala nafe Yehova,

Anene tsono Israyeli;

2 Akadapanda kukhala nafe Yehova,

Pakutiukira anthu:

3 Akadatimeza amoyo,

Potipsera mtima wao.

4 Akadatimiza madziwo,

Mtsinje ukadapita pa moyo wathu;

5 Madzi odzikuza akadapita pa moyo wathu.

6 Alemekezedwe Yehova,

Amene sanatipereka kumano kwao tikhale cakudya cao.

7 Moyo wathu unaonjoka ngati mbalame mu msampha wa msodzi;

Msampha unatyoka ndi ife tinaonioka.

8 Thandizo lathu liri m’dzina la Yehova,

Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.