Ayamikira mokondwerera kuti Mulungu anabweza ukapolo wao
Nyimbo yokwerera.
1 Pobweza Yehova ukapolo wa Ziyoni,
Tinakhala ngati anthu akulota.
2 Pamenepo pakamwa pathu panadzala ndi kuseka,
Ndi lilime lathu linapfuula mokondwera;
Pamenepo anati mwa amitundu,
Yehova anawacitira iwo zazikuru,
3 Yehova anaticitira ife zazikuru;
Potero tikhala okondwera.
4 Bwezani ukapolo wathu, Yehova,
Ngati mitsinje ya ku Mwera.
5 Akubzala ndi misozi adzatuta ndi kupfuula mokondwera.
6 Iye amene ayendayenda nalira, ponyamula mbeu yakufesa;
Adzabweranso ndithu ndi kupfuula mokondwera, alikunyamula mitolo yace.