Masalmo 127

Madalitso onse, a m’banja omwe, acokera kwa Mulungu

Nyimbo vokwerera; ya Solomo.

1 Akapanda kumanga nyumba Yehova,

Akuimanga agwiritsa nchito cabe;

Akapanda kusunga mudzi Yehoya,

Mlonda adikira cabe.

2 Kuli cabe kwa inu Rulawirira mamawa ndi kusagonerapo madzulo,

Kudya mkate wosautsa kuupeza;

Kuli tero kuti izi apatsa okondedwa ace ngati m’tulo.

3 Taonani ana ndiwo colandira ca kwa Yehova;

Cipatso ca m’mimba ndico mphotho yace.

4 Ana a ubwana wace wa munthu

Akunga mibvi m’dzanja lace la ciphona.

5 Wodala munthu amene anadzaza nayo phodo lace:

Sadzacita manyazi iwo,

Pakulankhula nao adani kucipata.