Masalmo 128

Wakuopa Yehova adalitsidwa m’banja mwace

Nyimbo yokwerera.

1 Wodala yense wakuopa Yehova, Wakuyenda m’njira zace.

2 Pakuti udzadya za nchito ya manja ako;

Wodala iwe, ndipo kudzakukomera.

3 Mkazi wako adzanga mpesa wopatsa m’mbali za nyumba yako;

Ana ako adzanga timitengo ta azitona pozinga podyera pako.

4 Taonani, m’mwemo adzadalitsika

Munthu wakuopa Yehova.

5 Yehova adzakudalitsa ali m’Ziyoni

Ndipo udzaona zokoma za Yerusalemu masiku onse a moyo wako.

6 Inde, udzaona zidzukulu zako.

Mtendere ukhale ndi Israyeli.