Masalmo 134

Afulumizidwa anthu kulemekeza Yehova

Nyimbo vokwerera,

1 Taonani, lemekezani Yehova, atumiki a Yehova inu nonse,

Akuimirira m’nyumba ya Yehova usiku,

2 Kwezani manja anu ku malo oyera,

Nimulemekeze Yehova.

3 Yehova, ali m’Ziyoni, akudalitseni;

Ndiye amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi.