Masalmo 137

Kudandaula kwa Ayuda ku Babulo

1 Ku mitsinje ya ku Babulo,

Kumeneko tinakhala pansi, inde tinalira,

Pokumbukila Ziyoni.

2 Pa msondodzi uli m’mwemo Tinapacika mazeze athu.

3 Popeza pamenepo akutigwirawo anatifunsa nyimbo,

Ndipo akutizunza anafuna tisekere,

Ndi kuti, Mutiyimbire nyimbo imodzi ya ku Ziyoni.

4 Tidati, Tidzayimba bwanji nyimbo ya Yehova

M’dziko lacilendo?

5 Ndikakuiwalani, Yerusalemu,

Dzanja lamanja langa liiwale luso lace.

6 Lilime langa limamatike ku nsaya zanga,

Ndikapanda kukumbukila inu;

Ndikapanda kusankha Yerusalemu

Koposa cimwemwe canga copambana.

7 Yehova, kumbukilani ana a Edomu

Tsiku la Yerusalemu;

Amene adati, Gamulani, gamulani,

Kufikira maziko ace.

8 Mwana wamkazi wa ku Babulo, iwe amene udzapasulidwa;

Wodala iye amene adzakubwezera cilango

Monga umo unaticitira ife.

9 Wodala iye amene adzagwira makanda ako,

Ndi kuwaphwanya pathanthwe.