Masalmo 138

Davide ayamika Mulungu pa kukhulupirika kwace, naneneratu kuti mafumu onse adzatero

Salmo la Davide.

1 Ndidzakuyamikani ndi mtima wangawonse;

Ndidzayimba zakukulemekezani patsogolo pa milungu,

2 Ndidzagwadira kuloza ku Kacisi wanu woyera,

Ndi kuyamika dzina lanu,

Cifukwa ca cifundo canu ndi coonadi canu;

Popeza munakuzitsa mau anu koposa dzina lanu lonse.

3 Tsiku loitana ine, munandiyankha,

Munandilimbitsa ndi mphamvu m’moyo mwanga.

4 Mafumu onse a pa dziko lapansi adzakuyamikani,

Yehova, popeza adamva mau a pakamwa panu.

5 Ndipo adzayimbira njira za Yehova;

Pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukuru.

6 Angakhale Yehova ngwokwezeka, apenyanso wopepukayo;

Koma wodzikuza amdziwira kutali.

7 Ndingakhale ndiyenda pakati pa nsautso, mudzandipatsa moyo;

Mudzatambasula dzanja lanu pa mkwiyo wa adani anu,

Ndipo dzanja lanu lamanja lidzandipulumutsa.

8 Yehova adzanditsirizira za kwa ine:

Cifundo canu, Yehova, cifikira ku nthawi zonse:

Musasiye nchito za manja anu.