Masalmo 140

Davide apempha Mulungu amlanditse kwa mdani woipa wamphamvu

Kwa Mkulu wa nsembe; Salmo la Davide.

1 Ndilanditseni, Yehova, kwa munthu woipa;

Ndisungeni kwa munthu waciwawa;

2 Amene adzipanga zoipa mumtima mwao;

Masiku onse amemeza nkhondo.

3 Anola lilime lao ngati njoka;

Pansi pa milomo yao pali ululu wa mphiri.

4 Ndilindireni Yehova, ndisalowe m’manja mwa woipa;

Ndisungeni kwa munthu waciwawa;

Kwa iwo akuti akankhe mapazi anga.

5 Odzikuzaanandichera msampha, nandibisira zingwe;

Anacha ukonde m’mphepete mwa njira;

Anandichera makwekwe.

6 Ndinati kwa Yehova, Inu ndinu Mulungu wanga;

Mundicherere khutu mau a kupemba kwanga, Yehova.

7 Yehova Ambuye, ndinu mphamvu ya cipulumutso canga,

Munandiphimba mutu wanga tsiku lakulimbana nkhondo.

8 Yehova, musampatse woipa zokhumba iye;

Musamthandize zodzipanga zace; angadzikuze.

9 Kunena za mutu wao wa iwo akundizinga,

Coipa ca milomo yao ciwaphimbe.

10 Makala amoto awagwere;

Aponyedwe kumoto;

M’maenje ozama, kuti asaukenso.

11 Munthu wamlomo sadzakhazikika pa dziko lapansi;

Coipa cidzamsaka munthu waciwawa kuti cimgwetse.

12 Ndidziwa kuti Yehova adzanenera wozunzika mlandu,

Ndi kuweruzira aumphawi,

13 Indedi, olungama adzayamika dzina lanu;

Oongoka mtima adzakhala pamaso panu,