Masalmo 141

Davide apempha Mulungu amthandize poyesedwa ndi zoipa

Salmo la Davide.

1 Yehova, ndaitana kwa Inu; ndifulumireni ine;

Mundicherere khutu, pamene ndiitana kwa Inu.

2 Pempherolanga liikike ngaticofukiza pamaso panu;

Kukweza manja anga kuikike ngati nsembe ya madzulo.

3 Muike mdindo pakamwa panga, Yehova;

Sungani pakhomo pa milomo yanga.

4 Mtima wanga usalinge ku cinthu coipa,

Kucita nchito zoipa

Ndi anthu akucita zopanda pace;

Ndipo ndisadye zankhuli zao.

5 Akandipanda munthu wolungama ndidzati ncifundo:

Akandidzudzula, ndidzakuyesa mafuta a pamutu;

Mutu wanga usakane:

Pakuti pangakhale posautsidwa iwo ndidzawapempherera.

6 Oweruza ao anagwetseka pambali pa thanthwe;

Nadzamva mau anga kuti ndiwo okondweretsa.

7 Mafupa athu amwazika pakamwa pa manda,

Monga ngati akumba nanyimphula nthaka yapansi.

8 Pakuti maso anga apenya kwanu, Yehova Ambuye;

Ndithawira kwa Inu; musataye moyowanga.

9 Mundisunge ndisagwe mumsampha anandicherawo,

Ndisakodwe m’makwekwe a iwo ocita zopanda pace,

10 Oipa agwe pamodzi m’maukonde ao,

Kufikira nditapitirira ine.