Masalmo 142

Pemphero pakuopsedwa kwakukuru

Cilangizo ca Davide, muja anakhala m’phanga; Pemphero,

1 Ndipfuula nalo liu langa kwa Yehova;

Ndi mau anga ndipemba kwa Yehova.

2 Nditsanulirakudandaulakwanga pamaso pace;

Ndionetsa msauko wanga pamaso pace.

3 Pamene mzimu wanga unakomoka m’kati mwanga, munadziwa njira yanga.

M’njira ndiyendamo anandichera msampha,

4 Penyani ku dzanja lamanja ndipo muone; palibe wondidziwa;

Pothawirapo pandisowa; palibe mmodzi wosamalira moyo wanga.

5 Ndinapfuulira kwa inu, Yehova;

Ndina, Inu ndinu pothawirapo panga,

Gawo langa m’dziko la amoyo.

6 Tamverani kupfuula kwanga; papeza ndisauka kwambiri;

Ndilanditseni kwa iwo akundilondola; popeza andilaka.

7 Turutsani moyo wanga m’ndende, kuti ndiyamike dzina lanu;

Olungama adzandizinga;

Pakuti mudzandicitira zokoma.