Masalmo 143

Davide apempha Mulungu amlanditse msanga kwa adani ace

Salmo la Davide.

1 Imvani pemphero langa, Yehova; ndicherere khutu kupemba kwanga;

Ndiyankheni mwa cikhulupiriko canu, mwa cilungamo canu.

2 Ndipo musaitane mlandu wa mtumiki wanu;

Pakuti pamaso panu sipadzakhala wolungama wamoyo mmodzi yense.

3 Pakuti mdani alondola moyo wanga;

Apondereza pansr moyo wanga;

Andikhalitsa mumdima monga iwo adafa kale lomwe.

4 Potero mzimu wanga wakomoka mwa ine;

Mtima wanga utenga nkhawa m’kati mwanga,

5 Ndikumbukila masiku a kale lomwe;

Zija mudazicita ndilingirirapo;

Ndikamba pa ndekha za nchito ya manja anu.

6 Nditambalitsira manja anga kwa Inu:

Moyo wanga ulira Inu monga dziko lolira mvula.

7 Fulumirani ndiyankheni, Yehova; mzimu wanga ukutha.

Musandibisire nkhope yanu;

Ndingafanane nao akutsikira kudzenje.

8 Mundimvetse cifundo canu mamawa;

Popeza ndikhulupirira Inu:

Mundidziwitse njira ndiyendemo;

Popeza ndikweza moyo wanga kwa Inu.

9 Mundilanditse kwa adani anga, Yehova;

Ndibisala mwa Inu.

10 Mundiphunzitse cokonda Inu; popeza Inu ndinu Mulungu wanga;

Mzimu wanu ndi wokoma; munditsogolere kucidikha.

11 Mundipatse moyo, Yehova, cifukwa ca dzina lanu;

Mwa cilungamo canu muturutse moyo wanga m’nsautso.

12 Ndipo mwa cifundo canu mundidulire adani anga,

Ndipo muononge onse akusautsa moyo wanga;

Pakuti ine ndine mtumiki wanu.